Ndani adapha Mwana woyamba kubadwa wa ku Igupto?

Anaika Novembala 13, 2020 ndi Danutasn Brown mu Pofotokoza Nkhani Zachiwawa za mu Baibulo

Ndani adapha Mwana woyamba kubadwa wa ku Igupto?

Anthu ena amaganiza kuti Mulungu ndiye wowononga, chifukwa pa Eksodo 12:29 akuti Mulungu “anakantha” oyamba kubadwa Aigupto. Mu Eksodo 12: 23 akuti “wowonongayo” adzalowa “mnyumba zanu kukantha.” Momwemo awiriwa ali ofanana; Mulungu = wowononga; zosavuta zedi sichoncho? Vuto ndirakuti Yesu akuti Iye ndiye “kuuka ndi moyo” [Yohane 11:25] ndipo mwa Khristu mulibe mdima konse [Yohane 1:5]. Khristu adapereka moyo wake “kuwononga iye ali ndi mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi” [Ahebri 2:14]. Ndipo kodi ndi Khristu yemweyo amene timamuyesa ngati wowononga yemwe amapita nyumba ndi nyumba kupha makanda?

Zenizeni ndizoti, Wowononga amatanthauza Satana:

             Ndipo linali nayo Mfumu yakulilamulira, mngelo wa phompho; dzina lace m’Cihebri Abadoni, ndi

             m’Cihelene ali nalo dzina Apoliyoni. [Apoliyoni amatanthauza “wowononga”]

             – Cibvumbulutso 9:11

Kodi Khristu ndiye “mngelo wa phompho wotchedwa Apoliyoni / Abadoni wowononga”

             Kapena tisayese Ambuye, monga ena a iwo anayesa, naonongeka ndi njoka zija. Kapena

             musadandaula, monga ena a iwo anadandaula, naonongeka ndi woonongayo.

             [1 Akorinto 10:9-10]

Mawu a wowononga pano mu Chihelene, malingana ndi Strong’s, ndi “njoka ya ululu.” Kodi Khristu ndi njoka ya ululu?

Komano tipanga bwanji kuti zimveke pa mfundo yonenanso kuti:

             Ndipo panakhala pakati pa usiku, Yehova anakantha ana oyamba onse m’dziko la Aigupto,

             kuyambira mwana woyamba wa Farao wakukhala pa mpando wacifumu wace kufikira mwana

             woyamba wa wam’nsinga ali m’kaidi; ndi ana woyamba onse a zoweta.  – Eksodo 12:29

M’chilankhulo cha Chiheberi Mulungu amanenedwa kuti amachita chirichonse, ngakhale sanachite ndiye molunjika. Mulungu nthawi zonse amatenga udindo pa chirichonse chifukwa ndiye Wamphamvu zonse, koma adalola kuti zichitike, atamuchenjeza mobwerezabwereza kuti akapanda kumvera, tsoka lidzagwera mtundu wake.

Werengani Eksodo 12:23 mosamala kachiwiri:

             Pakuti Yehova adzapita pakatipo kukantha Aaigupto; koma pamene adzaona mwaziwo pa

             mphuthu pamwamba ndi za pambali, Yehova adzapitirira pakhomopo, osalola woononga alowe

             m’nyumba zanu kukukanthani.

Mukayika mwazi wa mwana wa nkhosa pa khomo, Mulungu amatha kukutetezani kwa Satana. Sikuti Mulungu akukutetezani kwa Iye mwini. Ngati simumvera lamulo la Mulungu la momwe mungatetezeredwe, ndiye kuti simufuna chitetezo Chake. Ngati mtima wanu waumitsidwa kwathunthu kuti simukufuna kuchita kanthu ndi Mulungu, Iye amalemekeza ufulu wanu; choncho Mulungu auza mngelo wanu amene amakusamalirani kuti ayime.

Udindo ukadali pa ife kuti tisankhe. Izi zikufanana ndi funso loti ngati Mulungu adaumitsa mtima wa Farao kapena kodi Farao adaumitsa mtima wake? Mulungu adapereka chifundo ndi chisomo zomwe zidakanidwa, zidapangitsa kuumitsa. Motero mawu onsewa ndiowona.

Chitsanzo choyenera ndi chakuti ngati tinati kusuta ndudu kunamupha mwamunayo ndipo khansa idamupha. Sizitanthauza kuti kusuta = khansa; izi ndi zinthu ziwiri zosiyana. Koma kusuta kunamupha pomupatsa khansa. Titha kuwonjezera izi ndikuti mwamunayo adadzipha, koma sizitanthauza kuti mwamunayo = kusuta. Mulungu anakantha oyamba kubadwa mwa kulola Satana kukhala ndi ulamuliro pa mtunduwo; ndipo Satana amakondwera kupha ndi kuwononga, makamaka ngati anganene kuti Mulungu ndiye wachita. Kugwiritsa ntchito chilankhulochi ndikosiyana ndi momwe timamvetsetsera mawu wochita a verebu.

Nachi chitsanzo chomveka cha momwe Chiheberi chimanena kuti Mulungu amachita china chake molunjika, muchirankhulo cha Chingerezi, kuti Iye adalola kuti zichitike.

            “Ndipo tsopano taonani, Yehova waika mzimu wonama m’kamwa mwa aneneri anu onse awa,

            ndipo Yehova ananena coipa ca inu.” 1 Mafumu 22:23

Ponena za vesiri, kodi Mulungu adalamula mwachindunji mngelo wakugwa kuti apite kwa aneneri onyenga ndikunyenga Mfumu Sauli? Ayi, ziyenera kumvedwa ngati fanizo pomwe Mulungu amalola izi chifukwa cha zomwe Sauli adacita kuthamangitsa angelo abwino. Wolemba ndemanga wotchuka wa Baibulo, Adam Clakre, akunena izi pa vesiri:

            1 Mafumu 22:23 [Ambuye waika mzimu wabodza] Iye

            Walola kapena kuvutika ndi mzimu wonama kuti ukope aneneri ako. Kodi ndizofunikanso

            kukumbutsa wowerenga Malembo mobwerezabwereza kuti Mulungu akuchita chiyani, popereka

            chisamaliro chake, chimaloleza kapena kuvutika kuti chichitike? [zindikirani: Mulungu anati,

            “Sindidzalola kuti wowononga abwere m’nyumba zanu kukukanthani”]. Palibe chingachitike

            kumwamba, padziko lapansi, kapena ku gehena, koma mwina ndi mphamvu yake kapena

            chilolezo chake. Ichi ndi chifukwa chake Lemba likuyankhula pamwambapa.

Kumbukirani kuti Mulungu ali ndi mkangano ndi Satana. Anthu akamvera Satana, Satana amafuna akhale nzika zake monga momwe asankhila Satana. Satana amatsutsa Mulungu kuti amakakamiza kupezeka Kwake pa anthu amene safuna kutsogozedwa ndi Mulungu, Mzimu wake, kapena Chisomo chake. Mulungu podziwa mitima ya anthu ndi kulemekeza ufulu wawo wosankha, adzawalola kuti atsatire zofuna zawo ndikuvutitsidwa ndi Satana, pomwe nthawi zonse awayitana ndi mawu achifundo – “Ndikuthandizani, ngati mungandiyitane …… chonde itanani pa Ine,” akutero Mulungu. Koma kulamulidwa konse kwa Mulungu kumakanidwa, ndipo Mulungu amalola munthu kukolola chimene anafesa [Agalatiya 6:9].

Koma zikumbukiridwe kosatha ndi kufotokozedwa ndi Akhristu kuti chifundo cha Mulungu chimakhalapo kosatha [Masalmo 136], ndipo ngakhale titamukakhira kutali Mulungu, titha kulapa ndikuyitanira pa Iye.

            Ndipo ocita naye pamodzi tidandauliranso kuti musalandire cisomo ca Mulungu kwacabe inu,

            [pakuti anena, “M’nyengo yolandiridwa ndinamva iwe, Ndipo m’tsiku la cipulumutso

            ndinakuthandiza;” Taonani, tsopano ndiyo “nyengo yabwino” yolandiridwa, taonani, tsopano

            ndilo tsiku la Cipulumutso].  2 Akorinto 6:1-2