tatewachikondi.com

Timabuku

Kodi Inu Mumawerenga Bwanji?

Khristu amatiuza kuti Mawu a Mulungu ndi choonadi.

Koma pali zikhulupiriro zosiyanasiyana, ndipo mwachionekere zonsezo zimachokera m’Baibulo, choncho ife tingadziwe bwanji? Nanga tingadziwe bwanji choonadi pamene tikupeza kuti m’Baibulo muli zinthu zooneka ngati zotsutsana?

Baibulo lenilenilo limatiphunzitsa mmene tingathetsere mavuto wooneka ngati amenewa, mwa malangizo omveka bwino ndi mafanizo. Pamene ife tikutsatira malangizo a m’Malemba onena za mmene tingalandirire Mawu a Mulungu, kenako mmene timawerengera Baibulo zimasintha kwambiri. Paulo akutilangiza kugawa moyenera Mawu a choonadi - tingachite bwanji choncho?

Kuyankha mafunsowa, werengani m’kabukuka maziko a Mfundo Kapena Malamulo Omasulira, amene Baibulo limalengeza.

UTUMIKI WA KHRISTU KU DZIKO LAPANSI

Khristu anakweza khalidwe la Mulungu, kumpatsa Iye matamando, ndi kumpatsa Iye ulemu, ku cholinga chake chonse cha utumiki wake pa dziko lapansi, kukonza anthu kupyolera mu vumbulutso la Mulungu. Mwa Khristu adavekedwa pamaso pa anthu chisomo cha tate ndi  ungwiro wosayerekezeka wa Atate. Mu pemphero lake Iye asanapachikidwe, Iye analengeza, “Ine ndaliwonetsera dzina lanu.” “Ine ndakulemekezani pa dziko lapansi; Ine ndatsiriza ntchito imene munandipatsa Ine ndichite.” Pamene cholinga cha utumiki wake chinali chitakwaniritsidwa, ndicho chivumbulutso cha Mulungu ku dziko lapansi, —Mwana wa Mulungu analengeza kuti ntchito yake inakwaniritsidwa, ndikuti khalidwe la Atate linawonetseredwa kwa anthu. {Signs of the Times, January 20, 1890, par. 9}